10/04/2026
Lawyer Justice Nneneya walemba pa tsamba lake lanchezo kuti:
Amuna ambiri sadziwa izi pepani azibambo omwe munakwatira nkazi wamwana kale
Kukwatira mkazi amene ali kale ndi mwana. M'mamusamalira mwanayo, mumadyetsa, mumamulipirira sukulu, ndipo mumachita ngati ndinu bambo ake eni eni.
Koma choti muziwe tsiku lina, bambo enieni aja amene anali atasowa akadzabwera mwadzidzidzi, ngakhale iwo udindo anawuthawa mudzadabwa mukamva kuti: “Inu si bambo ovomerezeka pa malamulo a mwanayu, ndipo ndizoona or atazaphunzira chotani chifukwa Cha chuma chanu mwanayo sadzakhalabe wanu.
Inde, werengani kachiwiri.
Chikondi chanu chonse, ndalama, ndi nsembe zimene mumapereka kwa mwana ompeza sizimatanthauza kanthu pa malamulo, chifukwa mwanayo adzakhalabe wa bambo ake enieni omwe anathira batire ndikuphulitsa nkazi yemwe mulinaye inuyo pano pa malamulo.
Ndipo or nkhani mutazayitula ku Court kuti mwanayo waphunzira Sukulu chifukwa Cha ndalama zanu zanthumba abambo ake eni eni sanapelekeko chithandizo or 1 Kwacha izi pa court sizizamveka ndipo Mlandu umenewo mzaludzabe chifukwa inu nanu mwanayo mwachita chomupeza chabe ndipo Si wanu ndipo sadzakhala wanu ngakhale mwaononga ndalama zambili pa iye, pa Malamulo mwanayo ndimagazi a (Biological father) basi.
Eyatu Zikomo Azibambo omwe mukulera Ana oti Si anu👏